Prayers in Chewa | Dominik M. Ramík Dominik M. Ramík
Česky
En français


Prayers in Chewa (chicheŵa)

list Show the list of prayers in all languages





autorenewLoading the map
 Vigorous language (126)   Endangered language (12)   Moribund / extinct language (4)
 Speaker outside of the usual language range


Do you like this project? Support it by a donation via PayPal.

Chewa, Nyanja (chicheŵa)

face Speaker: Dominic (Malawi, Lilongwe)
add_circle_outline Church: Roman Catholic Church
translate Info about the language: text_fields Script: Latin (info on ScriptSource)
import_contacts Source of the text: The text comes from official church sources.

Sign of the Cross in Chewa (chicheŵa)

play_circle_filled
Mdzina la Atate, ndi la Mwana ndi la Mzimu Woyera. Amen

Lord's Prayer in Chewa (chicheŵa)

play_circle_filled
Atate athu muli m'mwamba,
dzina lanu liyeretsedwe,
ufumu wanu udze,
kufuna kwanu kuchitidwe,
monga kumwamba choncho pansi pano. 
Mutipatse ife lero chakudya chathu cha lero. 
Mutikhululukire ife zochimwa zathu,
monga ifenso tiakhululukira adani athu,
musatisiye ife m'chinyengo,
koma mutipulumutse ife kwa zoyipa.
Amen

Hail Mary in Chewa (chicheŵa)

play_circle_filled
Tikuoneni Maria wa chaulele chodzadza,
Ambuye ali nanu.
Ndinu odala kopambana akazi onse,
Ndipo mngodalanso mwana wanu Yesu.
Maria oyera amayi a mulungu
mutipempherere ife ochimwa,
Tsopano ndiponso pa nthawi yakufa kwathu.
Amen

Gloria Patri in Chewa (chicheŵa)

play_circle_filled
Ulemu ukhale kwa Atate, ndi kwa Mwana ndi kwa Mzimu Woyera,
monga panali poyamba ndi tsopano ndi masiku onse, ndi pa nthawi zosatha.
Amen

Apostles' Creed in Chewa (chicheŵa)

play_circle_filled
Ine ndimvera Mulungu Atate wamphamvu zonse,
amene analenga Dziko la kumwamba ndi dziko la pansi pano.
Ndipo Yesu Khristu Mwana wake yekha, Ambuye athu,
amene anayikidwa m'mimba ndi Mzimu Woyera,
nabadwa mwa Maria Virigo,
adamsautsa kwa Ponsio Pilato.
Adampachika pamtanda, anamwalira, adamuyika m'manda,
adalowa m'limbo, ndipo mkuja wake adauka kwa akufa,
nakwera kumwamba nakhala padzanja lamanja la Mulungu Atate Amphamvu zonse.
Adzafumira komweko kudzaweruza amoyo ndi akufa.
Ndipo ndimvera Mzimu Woyera,
Eklezia Katolika Woyera,
ndimveranso kuti Oyera ayanjana,
Mulungu atikhululukira machimo,
thupi lidzauka,
ulipo moyo osatha.
Amen
list Show the list of prayers in all languages



Madagaskar